Eksodo 9:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo m'mawa mwace Yehova anacita cinthuco, ndipo zinafa zoweta zonse za m'Aigupto; koma sicinafa cimodzi conse ca zoweta za ana a Israyeli.

7. Ndipo Farao anatuma, taonani, sicidafa cingakhale cimodzi comwe ca zoweta za Aisrayeli. Koma mtima wa Farao unauma, ndipo sanalola anthu amuke.

8. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Tengani phulusa la ng'anjo lodzala manja; ndi Mose aliwaze kuthambo pamaso pa Farao.

9. Ndipo lidzakhala pfumbi losalala pa dziko lonse la Aigupto, ndipo lidzakhala pa anthu ndi pa zoweta ngati zironda zobuka ndi matuza, m'dziko lonse la Aigupto.

Eksodo 9