Yeremiya 38:26-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. pamenepo uziti kwa iwo, Ndinagwa ndi pembedzero langa pamaso pa mfumu, kuti asandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani ndifere komweko.

27. Ndipo akuru onse anadza kwa Yeremiya, namfunsa; ndipo iye ananena nao monga mwa mau onsewo anamuuza mfumu. Ndipo analeka kunena naye; pakuti sikunamveka mlandu.

28. Ndipo Yeremiya anakhala m'bwalo la kaidi mpaka dzuwa lakugwidwa Yerusalemu. Ndipo anali komweko pogwidwa Yerusalemu.

Yeremiya 38