6. Ndipo ndidzakuponyera zonyansa, ndi kukucititsa manyazi, ndi kukuika copenyapo,
7. Ndipo kudzali kuti onse akupenyerera iwe adzakuthawa, nadzati, Nineve wapasuka, adzamlira maliro ndani? ndidzakufunira kuti akukutonthoza?
8. Kodi uli wabwino woposa No-Amoni, wokhala pakati pa mitsinje wozingidwa ndi madzi; amene chemba lace ndilo nyanja, ndi linga lace ndilo nyanja?
9. Kusi ndi Aigupto ndiwo mphamvu yace, ndiyo yosatha, Puti ndi Lubimu ndiwo akukuthandiza.
10. Koma iye anatengedwa, analowa ndende; ana ace a makanda anaphwanyika polekeza pace pa miseu yace yonse; ndi pa omveka ace anacita maere, ndi akulu ace onse anamangidwa maunyolo.
11. Iwenso udzaledzera, udzabisala; iwenso udzafunanso polimbikira cifukwa ca mdani.
12. Malinga ako onse adzanga mikuyu ndi nkhuyu zoyamba kupsa; akaigwedeza zingokugwa m'kamwa mwa wakudya.