Mlaliki 3:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndiponso kuti munthu yense adye namwe naone zabwino m'nchito zace zonse; ndiwo mtulo wa Mulungu.

14. Ndidziwa kuti zonse Mulungu azicita zidzakhala kufikira nthawi zonse; sungaonjezepo kanthu, ngakhale kucotsapo; Mulungu nazicita kuti anthu akaope pamaso pace.

15. Cocomwe cinaoneka, cirikuonekabe; ndi comwe cidzaoneka cinacitidwa kale; Mulungu anasanthula zocitidwa kale.

16. Ndiponso ndinaona kunja kuno malo akuweruza, komweko kuli zaipa; ndi malo a cilungamo, komweko kuli zoipa.

Mlaliki 3