Mateyu 21:42-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Yesu ananena kwa iwo, 1 Kodi simunawerenga konse m'malembo,Mwala umene anaukana omanga nyumbaWomwewu unakhala mutu wa pangondya:ici cinacokera kwa Ambuye,Ndipo ciri cozizwitsa m'maso mwathu?

43. Cifukwa cace ndinena kwa inu, 2 Ufumu wa Mulungu udzacotsedwa kwa inu, nudzapatsidwa kwa anthu akupatsa zipatso zace.

44. Ndipo 3 iye wakugwa pa mwala uwu adzaphwanyika; koma pa iye amene udzamgwera, udzampera iye.

45. Ndipo ansembe akuru ndi Afarisi, pakumva mafanizo ace, anazindikira kuti alikunena za iwo.

46. Ndipo pamene anafuna kumgwira, anaopa makamu a anthu, 4 cifukwa anamuyesa mneneri.

Mateyu 21