Luka 8:37-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Ndipo anthu aunyinji onse a dziko la Agerasa Ioyandikira anamfunsa iye acoke kwa iwo; cifukwa anagwidwa ndi mantha akuru. Ndipo iye analowa m'ngalawa, nabwerera.

38. Ndipo munthuyo amene ziwanda zinaturuka mwa iye anampempha iye akhale ndi iye; koma anamuuza apite, nanena,

39. Pita kunyumba kwako, nufotokozere zazikuruzo anakucitira iwe Mulungu. Ndipo iye anacoka, nalalikira ku mudzi wonse zazikuruzo Yesu anamcitira iye,

Luka 8