Genesis 8:2-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. ndipo anatsekedwa akasupe a madzi akuru ndi mazenera a kumwamba, niletsedwa mvula ya kwuwamba;

3. ndipo madzi anaphweraphwerabe pa dziko lapansi: pamene anatha masiku zana limodzi kudza makumi atatu madzi anacepa.

4. Ndipo cingalawa cinaima pa mapiri a Ararati, mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku lakhumi ndi asanu ndi awiri la mwezi.

5. Ndipo madzi analinkucepa kufikira mwezi wakhumi; mwezi wakhumi tsiku loyamba mwezi ndipo padaoneka mitu ya mapiri.

6. Ndipo panali atapita masiku makumi anai, Nowa anatsegula pa zenera la cingalawa limene analipanga:

7. ndipo anaturutsa khungubwe, ndipo anaturuka kunka kwina ndi kwina kufikira adaphwa madzi pa dziko lapansi,

8. Ndipo anaturutsa njiwa imcokere, kuti aone kapena madzi anaphwa pamwamba pa dziko lapansi;

9. koma njiwayo siinapeza popondapo phazi lace, nibwera kwa iye kucingalawako, pakuti madzi analipo pa dziko lonse lapansi; ndipo anaturutsa dzanja lace, naitenga, nailowetsa kwa iye m'cingalawamo.

10. Ndipo analinda masiku ena asanu ndi awiri; naturutsanso njiwayo m'cingalawamo;

11. ndipo njiwa inadza kwa iye madzulo; ndipo, taonani, m'kamwa mwace munali tsamba lazitona lotyoledwa: ndipo anadziwa Nowa kuti madzi analimkuphwa pa dziko lapansi.

12. Ndipo analindanso masiku ena asanu ndi awiri; naturutsa njiwayo: ndipo siinabweranso konse kwa iye.

Genesis 8