Ezekieli 40:48-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

48. Pamenepo anadza nane ku khonde la kacisi, nayesa mphuthu za khonde, mikono isanu cakuno, ndi mikono isanu cauko; ndi kupingasa kwa cipata, mikono itatu cakuno, ndi mikono itatu cauko.

49. M'litali mwace mwa khonde mikono makumi awiri, ndi kupingasa kwace mikono khumi ndi umodzi; ndipo panali makwerero khumi okwerera kumeneko; ndipo panali zoimiritsa pa nsanamirazo, imodzi cakuno, ndi imodzi cauko.

Ezekieli 40