1. Zitatha zinthu izi zokhulupirika, anadza Sanakeribu mfumu ya Asuri, nalowera Yuda, namangira midzi yamalinga misasa, nati adzigonjetsere iyi.
2. Ndipo pakuona Hezekiya kuti wadza Sanakeribu, ndi kuti nkhope yace inalunjikitsa kuyambana nkhondo ndi Yerusalemu,
3. anapangana ndi akuru ace ndi amphamvu ace, kutseka madzi a m'akasupe okhala kunja kwa mudzi; namthandiza iwo.
4. Nasonkhana anthu ambiri, natseka akasupe onse, ndi mtsinje woyenda pakati pa dziko, ndi kuti, Angafike mafumu a Asuri ndi kupeza madzi ambiri.
5. Ndipo analimbika mtima, namangitsa linga lonse mopasuka, nalikweza mpaka pansanja, ndi linga lina kunja kwace, nalimbitsa Milo m'mudzi wa Davide, napanga zida ndi zikopa zocuruka.