2 Mafumu 20:19-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Pamenepo Hezekiya anati kwa Yesaya, Mau a Yehova udawanena ndi abwino. Natinso, Si momwemo nanga, mtendere ndi coonaeli zikakhala masiku anga?

20. Macitidwe ena tsono a Hezekiya, ndi mphamvu yace yonse, ndi umo anamangira dziwe ndi mcera, nautengera mudzi madzi, sizilembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

21. Nagona Hezekiya ndi makolo ace; nakhala mfumu m'malo mwace Manase mwana wace.

2 Mafumu 20