2 Akorinto 5:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Koma zinthu zonse zicokera kwa Mulungu amene anatiyanjanitsa kwa iye yekha mwa Kristu, natipatsa utumiki wa ciyanjanitso;

19. ndiko kunena kuti Mulungu anali mwa Kristu, alinkuyanjanitsa dziko lapansi kwa Iyeyekha, osawawerengera zolakwa zao; ndipo anaikiza kwa ife mau a ciyanjanitso,

20. Cifukwa cace tiri atumiki m'malo mwa Kristu, monga ngati Mulungu alikudandaulira mwa ife; tiumiriza inu m'malo mwa Kristu, yanjanitsidwani ndi Mulungu,

21. Ameneyo sanadziwa ucimo anamyesera ucimo m'malo mwathu; kuti ife tikhale cilungamo ca Mulungu mwa iye.

2 Akorinto 5