1 Petro 2:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Cifukwa kwalembedwa m'lembo,Taona, ndiika m'Ziyoni mwala wotsiriza wa pangondya, wosankhika, wa mtengo wace;Ndipo wokhulupirira iye sadzanyazitsidwa.

7. Kwa inu tsono akukhulupira, ali wa mtengo wace; koma kwa iwo osakhulupira,Mwala umene omangawo anaukana,Womwewo unayesedwa mutu wa pangondya;

8. ndipo,Mwala wakukhumudwa nao, ndi thanthwe lopunthwitsa;kwa iwo akukhumudwa ndi mau, pokhala osamvera, kumenekonso adaikidwako.

9. Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe acifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mw ni wace, kotero kuti mukalakire zoposazo za iye amene anakuitanani muturuke mumdima, mulowe kuunika kwace kodabwitsa;

10. inu amene kale simunali anthu, koma tsopano muli anthu a Mulungu; amene kale simunalandira cifundo, koma tsopano mwalandira cifundo.

1 Petro 2