1 Mbiri 28:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Davide anasonkhanitsa ku Yerusalemu akalonga Israyeli, a akalonga a mapfuko, ndi akuru a zigawo zakutumikira mfumu, ndi akulu a zikwi, ndi akuru a mazana, ndi akuru a zolemera zonse, ndi zoweta zonse za mfumu, ndi ana ace; pamodzi ndi akapitao ndi anthu amphamvu, ndiwo ngwazi zamphamvu onsewo.

2. Ndipo mfumu Davide anaima ciriri, nati, Mundimvere ine, abale anga ndi anthu anga, ine kumtima kwanga ndinafuna kulimangira likasa la cipangano la Yehova, ndi popondapo mapazi a Mulungu wathu nyumba yopumulira, ndipo ndidakonzeratu za nyumbayi.

3. Koma Mulungu anati kwa ine, Sudzamangira dzina langa nyumba, popeza ndiwe munthu wa nkhondo wokhetsa mwazi.

1 Mbiri 28