Zekariya 9:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Katundu wa mau a Yehova pa dziko la Hadraki, ndipo Damasiko adzakhala popumula pace; pakuti Yehova apenyerera anthu monga apenyerera mafuko onse a Israyeli;

2. ndi Hamati yemwe wogundana naye malire; Turo ndi Zidoni, angakhale ali ndi nzeru zambiri.

3. Ndipo Turo adzadzimangira polimbikirapo, nadzakundika siliva ngati pfumbi, ndi golidi woyenga ngati thope la kubwalo.

4. Taonani, Yehova adzamlanda zace, nadzakantha mphamvu yace igwe m'manja; ndipo adzatha ndi moto.

5. Asikeloni adzaciona, nadzaopa; Gazanso, nadzanjenjemera kwambiri; ndi Ekroni, pakuti ciyembekezo cace cacitidwa manyazi; ndipo mfumu idzatayika ku Gaza, ndi Asikeloni adzasowa okhalamo.

6. Ndi mtundu wa anthu osokonezeka udzakhala m'Asidodi, ndipo ndidzaononga kudzikuza kwa Afilisti.

Zekariya 9