1. Ndipo ndinakwezanso maso anga, ndinapenya, ndipo taonani, anaturuka magareta anai pakati pa mapiri awiri; ndi mapiriwo ndiwo mapiri amkuwa.
2. Ku gareta woyamba kunali akavalo ofiira; ndi ku gareta waciwiri akavalo akuda;
3. ndi ku gareta wacitatu akavalo oyera; ndi ku gareta wacinai akavalo olimba amawanga.