Zekariya 6:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ndinakwezanso maso anga, ndinapenya, ndipo taonani, anaturuka magareta anai pakati pa mapiri awiri; ndi mapiriwo ndiwo mapiri amkuwa.

2. Ku gareta woyamba kunali akavalo ofiira; ndi ku gareta waciwiri akavalo akuda;

3. ndi ku gareta wacitatu akavalo oyera; ndi ku gareta wacinai akavalo olimba amawanga.

Zekariya 6