Zekariya 4:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mthengayo adalankhula nane, anadzanso, nandiutsa ngati munthu woutsidwa m'tulo tace.

2. Ndipo anati kwa ine, Uona ciani? Ndipo ndinati, Ndaona, taonani, coikapo nyali ca golidi yekha yekha, ndi mbale yace pamwamba pace, ndi nyali zace zisanu ndi ziwiri pamenepo; nyalizo zinali ndi misiwe isanu ndi iwiri, ndiyo ya nyalizo zinali pamwamba pace;

3. ndi mitengo iwiri yaazitona pomwepo, wina ku dzanja lamanja la mbaleyo, ndi wina ku dzanja lace lamanzere.

Zekariya 4