Zekariya 14:5-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pamenepo mudzathawa kudzera cigwa ca mapiri anga; pakuti cigwa ca mapiri cidzafikira ku Azali; ndipo mudzathawa monga umo munathawira cibvomezi, masiku a Uziya mfumu ya Yuda; ndipo Yehova Mulungu wanga adzadza, ndi opatulika onse pamodzi ndi Inu.

6. Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo, sikudzakhala kuunika, zowalazo zidzada;

7. koma lidzakhala tsiku la pa lokha lodziwika ndi Yehova; palibe usana, palibe usiku; koma kudzatero kuti madzulo kudzati mbe.

Zekariya 14