1. Taonani likudza tsiku la Yehova, limene zofunkha zako zidzagawanika pakati pako.
2. Pakuti ndidzasonkhanitsa amitundu onse alimbane ndi Yerusalemu; ndipo mudziwo udzalandidwa, ndi nyumba zidzafunkhidwa, ndi akazi adzakakamizidwa; ndi limodzi la magawo awiri la mudzi lidzaturuka kumka kundende, koma anthu otsala sadzaonongeka m'mudzimo.
3. Pamenepo Yehova adzaturuka, nadzacita nkhondo ndi amitundu aja, monga anacitira nkhondo tsiku lakudumana.