Yoweli 2:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Atumphako ngati mkokomo wa magareta pamwamba pa mapiri, ngati kulilima kwa malawi a moto akupsereza ziputu, ngati mtundu wamphamvu wa anthu ondandalikira nkhondo.

6. Pamaso pao mitundu ya anthu ikumva zowawa, nkhope zonse zitumbuluka.

7. Athamanga ngati amphamvu; akwera linga ngati anthu a nkhondo; niliyenda liri lonse njira yace, osasokonezeka m'mabande ao.

8. Sakankhana, ayenda liri lonse m'mopita mwace; akagwa m'zida, siityoka nkhondo yao.

9. Alumphira mudzi, athamanga palinga, akwerera nyumba, alowera pamazenera ngati mkhungu.

10. Dziko lapansi linjenjemera pamaso pao, thambo ligwedezeka, dzuwa ndi mwezi zada, ndi nyenyezi zi'bweza kuwala kwao;

11. ndipo Yehova amveketsa mau ace pamaso pa khamu lace la nkhondo; pakuti a m'cigono mwace ndi ambirimbiri; pakuti Iye wakucita mau ace ndiye wamphamvu ndithu; pakuti tsiku la Yehova ndi lalikuru ndi loopsa ndithu; akhoza kupirira nalo ndani?

Yoweli 2