24. Ndipo anamyankha Yoswa nati, Popeza anatiuzitsa akapolo anu kuti Yehova Mulungu wanu analamulira mtumiki wace Mose kukupatsani dziko lonseli, ndi kupasula nzika zonse za m'dziko pamaso panu; potero tinaopera kwambiri moyo wathu pamaso panu, ndipo tinacita cinthuci.
25. Ndipo tsopano, taonani, tiri m'dzanja lanu; monga muyesa cokoma ndi coyenera kuticitira ife, citani.
26. Pamenepo anawacitira cotero, nawalanditsa m'dzanja la ana a Israyeli, angawaphe.