Yoswa 8:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Nauka msanga olalirawo m'mbuto mwao, nathamanga pamene anatambasula dzanja lace, nalowa m'mudzi, naugwira; nafulumira nayatsa mudziwo.

20. Pamene amuna a ku Ai anaceuka, anapenya, ndipo taonani, utsi wa mudzi unakwera kumwamba; nasowa mphamvu iwo kuthawa cakuno kapena cauko; ndi anthu othawira kucipululu anatembenukira owapitikitsa.

21. Ndipo pakupenya Yoswa ndi Israyeli yense kuti olalirawo adagwira mudzi, ndi kuti utsi wa mudzi unakwera, anabwerera, nawapha amuna a ku Ai.

22. A kumudzinso anawaturukira; potero anakhala pakati pa Israyeli, ena mbali yina, ena mbali yina; ndipo anawakantha, mpaka sanatsala kapena kupulumuka wa iwo ndi mmodzi yense.

Yoswa 8