Yoswa 6:9-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo okonzeka kunkhondo anatsogolera ansembe akuliza mphalasa, koma akudza m'mbuyo anatsata likasa, ansembe ali ciombere poyenda iwo.

10. Ndipo Yoswa analamulira anthu, ndi kuti, Musamapfuula, kapena kumveketsa mau anu, asaturuke konse mau m'kamwa mwanu, mpaka tsiku lakunena nanu ine, Pfuulani; pamenepo muzipfuula.

11. Ndipo anazungulitsa likasa la Yehova mudzi, kuzungulira kamodzi; pamenepo analowa kucigono, nagona m'mwemo.

Yoswa 6