10. Ndipo ana a Israyeli anamanga misasa ku Giligala; nacita Paskha tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi, madzulo, m'zidikha za Yeriko.
11. Ndipo m'mawa mwace atatha Paskha, anadya tirigu wakhwimbi wa m'dziko, mikate yopanda cotupitsa ndi tirigu wokazinga tsiku lomwe lija.
12. Koma m'mawa mwace mana analeka, atadya iwo tirigu wakhwimbi wa m'dziko; ndipo ana a Israyeli analibenso mana; koma anadya zipatso za dziko la Kanani caka comwe cija.