14. Tsiku lomwelo Yehova anakulitsa Yoswa pamaso pa Aisrayeli onse; ndipo anamuopa monga anaopa Mose, masiku onse amoyowace.
15. Ndipo Yehova anati kwa Yoswa,
16. Lamulira ansembe akusenza likasa la umboni, kuti akwere kuturuka m'Yordano.
17. Pamenepo Yoswa analamulira ansembe, ndi kuti, Kwerani kuturuka m'Yordano.