Yoswa 17:4-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo anayandikira pamaso pa Eleazare wansembe, ndi pamaso pa Yoswa mwana wa Nuni, ndi pamaso pa akalonga, ndi kuti, Yehova analamulira Mose atipatse colowa pakati pa abale athu; cifukwa cace anawapatsa monga mwa lamulo La Yehova, colowa pakati pa abale a atate wao.

5. Ndipo anamgwera Manase magawo khumi, osawerenga dziko la Gileadi ndi Basana lokhala tsidya lija la Yordano:

6. popeza ana akazi a Manase adalandira colowa pakati pa ana ace amuna; ndi dziko la Gileadi linakhala la ana a Manase otsala.

Yoswa 17