Yoswa 16:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. naturuka malire kumadzulo ku Mikametatu kumpoto; nazungulira malire kum'mawa kumka ku Taanatu-silo, naupitirira kum'mawa kwace kwa Yanoa:

7. natsika kucokera ku Yanoa, kumka ku Atarotu, ndi ku Naara, nafika ku Yeriko, naturuka ku Yordano.

8. Kuyambira ku Tapua malire anamuka kumadzulo ku mtsinje wa Kana; ndi maturukiro ace anali kunyanja. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Efraimu monga mwa mabanja ao;

9. pamodzi ndi midzi adaipatulira ana a Efraimu pakati pa colowa ca ana a Manase, midzi yonse pamodzi ndi miraga yao.

10. Ndipo a sanaingitsa Akanani akukhala m'Gezeri; koma Akanani anakhala pakati pa Efraimu, kufikira lero lino, nawasonkhera msonkho.

Yoswa 16