Yoswa 11:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Motero Yoswa analanda dziko lonselo, la kumapiri, ndi la kumwera, ndi dziko lonse la Goseni, ndi dziko la kucidikha, ndi la kucigwa; ndi la kwnapiri la Israyeli, ndi la ku cidikha cace;

17. kuyambira phiri la Halaki lokwera kumka ku Seiri, mpaka Baala-gadi m'cigwa ca Lebano patsinde pa phiri la Herimoni; nagwira mafwnu ao onse, nawakantha, nawapha.

18. Yoswa anathira nkhondo mafwnu awa onse nthawi yaikuru.

19. Palibe mudzi wakupangana mtendere ndi ana a Israyeli, koma Ahivi okhala m'Gibeoni; anaigwira yonse ndi nkhondo.

Yoswa 11