Yoswa 10:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo Yoswa anati, Kunkhunizirani miyala yaikuru kukamwa kwa phanga, ndi kuikapo anthu, awasunge;

19. koma inu musaime, pitikitsani adani anu, ndi kukantha a m'mbuyo mwao; musawalole alowe m'midzi mwao; pakuti Yehova Mulungu wanu anawapereka m'dzanja lanu.

20. Ndipo kunali, Yoswa ndi ana a Israyeli atatha kuwakantha, makanthidwe akurukuru mpaka atatha psiti, ndipo otsala a iwo atalowa m'midzi ya malinga,

21. anthu onse anabwerera kucigono kwa Yoswa pa Makeda ndi mtendere. Palibe munthu anacitira cipongwe mmodzi yense wa ana a Israyeli.

22. Pamenepo Yoswa anati, Tsegula pakamwa pa phanga ndi kunditurutsira m'phanga mafumu asanuwo.

Yoswa 10