Yona 1:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Tsono anati kwa iye, Ticitenji nawe, kuti nyanja iticitire bata? popeza namondwe anakula-kulabe panyanja.

12. Ndipo anati nao, Mundinyamule ndi kundiponya m'nyanja, momwemo nyanja idzacitira inu bata; pakuti ndidziwa kuti namondwe wamkuru amene wakugwerani cifukwa ca ine.

13. Koma amunawo anapalasa kubwerera kumtunda, koma sanathe; pakuti namondwe wa panyanja anakulakula mokomana nao.

14. Pamenepo anapfuulira kwa Yehova, nati, Tikupemphanitu, Yehova, tisatayike cifukwa ca moyo wa munthu uyu, musatisenzetse mwazi wosacimwa; pakuti, Inu Yehova, mwacita monga mudakomera Inu.

15. Momwemo ananyamula Yona, namponya m'nyanja; ndipo nyanja inaleka kukokoma kwace.

Yona 1