Yohane 7:44-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. Koma 6 ena mwa iwo anafuna kumgwira iye; koma palibe munthu anamgwira kumanja.

45. Pamenepo anyamatawo anadza kwa ansembe akulu ndi Afarisi; ndipo iwowa anati kwa iwo, Simunamtenga iye bwanji?

46. Anyamatawo anayankha, 7 Nthawi yonse palibe munthu analankhula cotero.

47. Pamenepo Afarisi anayankha iwo, Kodi mwasokeretsedwa inunso?

48. 8 Kodi wina wa akuru anakhulupirira iye, kapena wa Afarisi?

Yohane 7