1. Zitapita izi anacoka Yesu kunka ku tsidya lija la nyanja ya Galileya, ndiyo ya Tiberiya,
2. Ndipo khamu lalikuru la anthu linamtsata iye, cifukwa anaona zizindikilo zimene anacita pa odwala.
3. Koma Yesu anakwera kuphiri, nakhala pansi komweko pamodzi ndi akuphunzira ace.