Yohane 4:37-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Pakuti m'menemo conenaco ciri coona, Wofesa ndi wina, womweta ndi winanso.

38. Ine ndinatuma inu kukamweta cimene simunagwirirapo nchito: ena anagwira nchito, ndipo inu mwalowa nchito yao.

39. Ndipo m'mudzi mula anthu Asamariya ambiri anamkhulupirira iye cifukwa ca mau a mkazi, wocita umboniyo, kuti, Anandiuza ine zinthu ziri zonse ndinazicita.

40. Cifukwa cace pamene Asamariya anadza kwa iye, anamfunsa akhale nao; ndipo anakhala komweko masiku awiri.

Yohane 4