4. Yesu nanena naye, Mkazi, ndiri ndi ciani ndi inu? nthawi yanga siinafike.
5. Amace ananena kwa atumiki, Cimene ciri conse akanena kwa inu, citani.
6. Ndipopanali pamenepo mitsuko yamiyala isanu ndi umodzi yoikidwako monga mwa mayeretsedwe a Ayuda, yonse ya miyeso iwiri kapena itatu.
7. Yesu ananena nao, Dzazani mitsukoyo ndi madzi. Naidzaza, nde nde nde.