Yohane 17:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Monga momwe munandituma Ine ku dziko lapansi, Inenso ndinatuma iwo ku dziko lapansi,

19. Ndipo cifukwa ca iwo Ine ndidzipatula ndekha kuti iwonso akhale opatulidwa m'coonadi.

20. Koma sindipempherera iwo okha, komanso iwo akukhulupirira Ine cifukwa ca mau ao;

21. kuti onse akakhale amodzi, monga Inu Atate mwa Ine, ndi Ine mwa Inu, kuti iwonso akakhale mwa Ife: kuti dziko lapansi likakhulupire kuti Inu munandituma Ine.

Yohane 17