14. Ngati mudzapempha kanthu m'dzina langa, ndidzacita.
15. Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.
16. Ndipo Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani inu Nkhoswe yina, kuti akhale ndi inu ku nthawi yonse,
17. ndiye Mzimu wa coonadi; amene dziko lapansi silingathe kumlandira, pakuti silimuona iye, kapena kumzindikira iye. Inu mumzindikira iye; cifukwa akhala ndi inu nadzakhala mwa inu.
18. Sindidza-kusiyani inu mukhale ana amasiye; ndidza kwa inu.