Yobu 9:7-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Amene alamulira dzuwa ndipo silituruka,Nakomera nyenyezi cizindikilo cakuzitsekera.

8. Woyala thambo yekha,Naponda pa mafunde a panyanja.

9. Wolenga Mlalang'amba, Akamwiniatsatana, ndi Nsangwe,Ndi Kumpotosimpita,

10. Wocita zazikuru zosasanthulika,Ndi zodabwiza zosawerengeka,

11. Taona, Mulungu apita pali ine, koma sindimpenya;Napitirira, koma osamaindikira ine.

12. Taona, akwatula, adzambwezetsa ndani?Adzanena naye ndani, Mulikucita ciani?

13. Mulungu sadzabweza mkwiyo wace;Athandizi odzikuza awerama pansi pa Iye.

14. Nanga ine tsono ndidzamyankha bwanji,Ndi kusankha mau anga akutsutsana ndi Iye?

15. Ameneyo, cinkana ndikadakhala wolungama, sindikadamyankha; Ndikadangompembedza wondiweruza ine.

16. Ndikadaitana, ndipo akadayankha Iye,Koma sindikadakhulupirira kuti Iye wamvera mau anga,

17. Pakuti andityola ndi mkuntho,Nacurukitsa mabala anga kopanda cifukwa.

Yobu 9