Yobu 9:27-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndikati, Ndidzaiwala condidandaulitsa,Ndidzasintha nkhope yanga yacisoni, ndidzasekerera;

28. Pamenepo ndiopa zisoni zanga zonse,Ndidziwa kuti simudzandiyesa wosacimwa.

29. Mlandu udzanditsutsa;Potero ndigwire nchito cabe cifukwa ninji?

30. Ndikasamba madzi a cipale cofewaNdi kuyeretsa manja anga ndi sopo;

31. Mudzandibviikanso muli zoola,Ndi zobvala zanga zidzanyansidwa nane.

32. Pakuti sindiye munthu, monga ine, kuti ndimyankhe,Kuti tikomane mlandu.

Yobu 9