Yobu 6:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Amada cifukwa ca madzi oundana.M'menemo cipale cofewa cibisika;

17. Atafikira mafundi, mitsinje iuma;Kukatentha, imwerera m'malo mwao.

18. Aulendo akutsata njira yao apambukapo,Akwerera poti se, natayika.

19. Aulendo a ku Tema anapenyerera,Makamu a ku Seba anaiyembekezera.

20. Anazimidwa popeza adaikhulupirira;Anafikako, nathedwa nzeru.

21. Pakuti tsopano mukhala mamwemo;Muona coopsa, mucitapo mantha.

Yobu 6