3. Ndinapenya wopusa woyala mizu;Koma pomwepo ndinatemberera pokhala pace.
4. Ana ace akhala otekeseka, Napsinjika kucipata,Wopanda wina wakuwapulumutsa.
5. Zokolola zao anjala azidya,Azitenga ngakhale kuminga,Ndi aludzu ameza cuma cao.
6. Pakuti nsautso siituruka m'pfumbi,Ndi mabvuto saphuka m'nthaka;