Yobu 5:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Pakuti udzakhala ndi pangano ndi miyala ya kuthengo;Ndi nyama za kuthengo zidzakhala nawe mumtendere.

24. Ndipo udzapeza kuti pahema pako mpa mtendere;Nudzazonda za m'banja mwako osasowapo kanthu,

25. Udzapezanso kuti mbeu zako zidzacuruka,Ndi obala iwe ngati zitsamba za padziko.

26. Udzafika kumanda utakalamba,Monga abwera nao mtolo wa tirigu m'nyengo yace.

Yobu 5