23. Pakuti udzakhala ndi pangano ndi miyala ya kuthengo;Ndi nyama za kuthengo zidzakhala nawe mumtendere.
24. Ndipo udzapeza kuti pahema pako mpa mtendere;Nudzazonda za m'banja mwako osasowapo kanthu,
25. Udzapezanso kuti mbeu zako zidzacuruka,Ndi obala iwe ngati zitsamba za padziko.
26. Udzafika kumanda utakalamba,Monga abwera nao mtolo wa tirigu m'nyengo yace.