Yobu 5:18-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pakuti apweteka, namanganso mabala;Alasa, ndi manja ace omwe apoletsa.

19. Adzakupulumutsa m'masautso asanu ndi limodzi;Cinkana mwa asanu ndi awiri palibe coipa cidzakukhudza.

20. Adzakuombola kuimfa m'njala,Ndi ku mphamvu ya lupanga m'nkhondo.

21. Udzabisikira mkwapulo wa lilime,Sudzaciopanso cikadza cipasuko.

22. Cipasuko ndi njala udzaziseka;Ngakhale zirombo za padziko osaziopa.

23. Pakuti udzakhala ndi pangano ndi miyala ya kuthengo;Ndi nyama za kuthengo zidzakhala nawe mumtendere.

24. Ndipo udzapeza kuti pahema pako mpa mtendere;Nudzazonda za m'banja mwako osasowapo kanthu,

Yobu 5