15. Apulumutsa aumphawi ku lopangaLa kukamwa kwao, ndi ku dzanja la wamphamvu.
16. Potero aumphawi ali naco ciyembekezo,Ndi mphulupulu yatsekedwa pakamwa.
17. Taona, wodala munthu amene Mulungu amdzudzula;Cifukwa cace usapeputsa kulanga kwa Wamphamvuyonse.
18. Pakuti apweteka, namanganso mabala;Alasa, ndi manja ace omwe apoletsa.
19. Adzakupulumutsa m'masautso asanu ndi limodzi;Cinkana mwa asanu ndi awiri palibe coipa cidzakukhudza.
20. Adzakuombola kuimfa m'njala,Ndi ku mphamvu ya lupanga m'nkhondo.
21. Udzabisikira mkwapulo wa lilime,Sudzaciopanso cikadza cipasuko.
22. Cipasuko ndi njala udzaziseka;Ngakhale zirombo za padziko osaziopa.
23. Pakuti udzakhala ndi pangano ndi miyala ya kuthengo;Ndi nyama za kuthengo zidzakhala nawe mumtendere.
24. Ndipo udzapeza kuti pahema pako mpa mtendere;Nudzazonda za m'banja mwako osasowapo kanthu,
25. Udzapezanso kuti mbeu zako zidzacuruka,Ndi obala iwe ngati zitsamba za padziko.