2. Kodi ukhoza kumanga m'mphuno ndi mlulu?Kapena kuboola nsagwada wace ndi momba?
3. Kodi idzacurukitsa mau akukupembedza?Kapena idzanena nawe mau ofatsa?
4. Kodi idzapangana ndi iwe,Kuti uitenge ikhale kapolo wako wacikhalire?
5. Kodi udzasewera nayo ngati mbalame?Kapena udzaimangira anamwali ako kuti aiwete?
6. Kodi opangana malonda adzaitsatsa?Adzaigawana eni malonda?