Yobu 40:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Yehova anamyankha Yobu m'kabvumvulu, nati,

7. Dzimangire m'cuuno tsono ngati mwamuna;Ndidzakufunsa, undidziwitse.

8. Cingakhale ciweruzo canga udzacityola kodi?Udzanditsutsa kuti ndiri woipa kodi, kuti ukhale wolungama ndiwe?

9. Kodi uli nalo dzanja ngati Ine Mulungu?Kapena ukhoza kugunda ndi mau ngati Ine?

10. Udzikometsere tsono ndi ukulu ndi kukuzika,Nubvale ulemu ndi ulemerero.

Yobu 40