Yobu 4:9-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Atayika ndi mpweya wa Mulungu,Nathedwa ndi mpumo wa mkwiyo wace.

10. Kubangula kwa mkango, ndi kulira kwa mkango waukali kwaletsedwa,Ndi mano a misona ya mkango atyoledwa.

11. Mkango wokalamba udzifera posowa mkoka,Ndi misona ya mkango waukazi imwazika.

12. Anditengera mau m'tseri,M'khutu mwanga ndinalandira kunong'oneza kwace.

13. M'malingaliro a masomphenya a usiku,Powagwira anthu tulo tatikuru,

14. Anandidzera mantha ndi kunjenjemera,Nanthunthumira nako mafupa anga onse.

15. Pamenepo panapita mzimu pamaso panga;Tsitsi la thupi langa lidati nyau nyau.

16. Unaima ciriri, koma sindinatha kuzindikira maonekedwe ace;Panali mzukwa pamaso panga;Kunali cete, ndipo ndidamva mau akuti,

17. Kodi munthu adzakhala wolungama ndi kuposa Mulungu?Kodi munthu adzakhala woyera woposa Mlengi wace?

Yobu 4