1. Kodi udziwa nyengo yakuswana zinkhoma?Kodi wapenyerera pakuswa nswala?
2. Ukhoza kodi kuwerenga miyezi yakuzipitira,Kapena udziwa nyengo yoti ziswane?
3. Zithuntha, ziswa,Zitaya zowawa zao.
4. Ana ao akhala ojinca, akulira kuthengo,Acoka osabwerera kwa amao.
5. Ndani walola mbidzi ituruke yaufulu?Anaimasulira mbidzi nsinga zace ndani,