Yobu 37:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Kodi mudziwa umo zobvala zanu zifundira,Pamene dziko liri thuu cifukwa ca mwela?

18. Kodi muyala thambo pamodzi ndi Iye,Ndilo lolimba ngati kalirole woyengeka?

19. Mutilangize cimene tidzanena ndi Iye;Sitidziwa kulongosola mau athu cifukwa ca mdima.

20. Kodi munthu ayenera kumuuza kuti ndifuna kunena,Kapena kodi munthu adzakhumba kumezedwa?

Yobu 37