5. Taonani, Mulungu ndiye mwini mphamvu, ndipo sapeputsa munthu;Mphamvu ya nzeru zace ndi yaikuru.
6. Sasunga woipa akhale ndi moyo,Koma awaninkha ozunzikazowayenera iwo.
7. Sawacotsera wolungama maso ace,Koma pamodzi ndi mafumu pa mpando waoAwakhazika cikhazikire, ndipo akwezeka.
8. Ndipo akamangidwa m'nsinga,Nakakodwa ndi zingwe za mazunzo,
9. Pamenepo awafotokozera nchito zao,Ndi zolakwa zao, kuti anacita modzikuza.