3. Ndidzatenga nzeru zanga kutali,Ndidzabvomereza kuti Mlengi wanga ndi wolungama.
4. Pakuti zoonadi, mau anga sali abodza,Wakudziwitsa mwangwiro ali nanu.
5. Taonani, Mulungu ndiye mwini mphamvu, ndipo sapeputsa munthu;Mphamvu ya nzeru zace ndi yaikuru.
6. Sasunga woipa akhale ndi moyo,Koma awaninkha ozunzikazowayenera iwo.
7. Sawacotsera wolungama maso ace,Koma pamodzi ndi mafumu pa mpando waoAwakhazika cikhazikire, ndipo akwezeka.