Yobu 34:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Popeza anapambuka, naleka kumtsata,Osasamalira njira zace ziri zonse.

28. M'mwemo anafikitsa kwa Iye kupfuula kwa osauka;Ndipo anamva Iye kupfuula kwa ozunzika.

29. Iye akapatsa mpumulo adzamtsutsa ndani?Akabisa nkhope yace adzampenyerera ndani?Cikacitika pa mtundu wa anthu, kapena pa munthu, ncimodzimodzi;

30. Kuti munthu wonyoza Mulungu asacite ufumu,Ndi anthu asakodwe mumsampha,

31. Pakuti pali wina kodi anati kwa Mulungu,Ndasenza kulanga kwanu, ndingakhale sindinalakwa?

Yobu 34